Mtsogoleri wa Chipani chatsopano mdziko muno Cha Malawian Dream Party (MDP) Musa Zalira wauza nyumba zofalitsa nkhani kuti chidzapambana pachisankho cha chaka chino.
Iye wati chipani chawo chibwerenzetsa chikhulupiliro Cha anthu ambiri maka achinyanata.
Chipani cha MDP chati chilembetsa mu kaundula wa zipani mwezi uno usanathe ndipo chipanga mgwirizano ndi zipani zokhazo zimene zikuyika achimata patsogolo.
Katswiri pa nkhani za ndale wonderful Mkhuche wati akukaika ngati chipanichi chikhale ndi nthawi yozigulitsila poti kwangotsala miyezi isanu ndi iwiri (7) kuti dziko lino lichititae chisankho mu mwezi wa Seputambala pa 16.
Masiku apitawa guru lina linayambiysanso chipani china Cha National Youth Alliance ndipo akuti ndi cha achinyanata.
(Daire Media Group)

Comments
Post a Comment